Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 51:22-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. ndi iwe ndidzatyolatyola gareta ndi iye wokweramo; ndi iwe ndidzatyolatyola mwamuna ndi mkazi; ndi iwe ndidzatyolatyola wokalamba ndi mnyamata; ndi iwe ndidzatyolatyola mnyamata ndi namwali;

23. ndi iwe ndidzatyolatyola mbusa ndi zoweta zace; ndi iwe ndidzatyolatyola wakulima ndi gori la ng'ombe lace; ndi iwe ndidzatyolatyola akazembe ndi ziwanga,

24. Ndipo ndidzabwezera Babulo ndi okhala m'Kasidi zoipa zao zonse anazicita m'Ziyoni pamaso panu, ati Yehova.

25. Taona, ndimenyana ndi iwe, iwe phiri lakuononga, ati Yehova, limene liononga dziko lonse; ndipo ndidzakutambasulira iwe dzanja langa, ndipo ndidzakugubuduza iwe kumatanthwe, ndipo ndidzakuyesa iwe phiri lotenthedwa.

26. Ndipo sadzacotsa pa iwe mwala wa pangondya, kapena mwala wa pamaziko; koma udzakhala bwinja nthawi zonse, ati Yehova.

27. Kwezani mbendera m'dziko, ombani lipenga mwa amitundu, konzerani amitundu amenyane naye, mummemezere maufumu a Ararati, Mini, ndi Asikenaza; muike nduna; amenyane naye; mukweretse akavalo ngati mandowa.

28. Konzerani amitundu amenyane ndi iye, mafumu a Amedi, akazembe ace, ndi ziwanga zace zonse, ndi dziko lonse la ufumu wace.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 51