Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 5:19-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo padzakhala: pamene mudzati, Cifukwa canji Yehova Mulungu wathu aticitira ife zonse izi? ndipo udzayankha kwa iwo, Monga ngati mwandisiya Ine, ndi kutumikira milungu yacilendo m'dziko lanu, momwemo mudzatumikira alendo m'dziko siliri lanu.

20. Nenani ici m'nyumba ya Yakobo, lalikirani m'Yuda, kuti,

21. Tamvanitu ici, inu anthu opusa, ndi opanda nzeru; ali ndi maso koma osaona, ali ndi makutu koma osamva;

22. Kodi simundiopa Ine? ati Yehova: simudzanthunthumira pamaso pa Ine, amene ndinaika mcenga cilekaniro ca nyanja, ndi lemba lamuyaya kuti isapitirirepo? ndipo ngakhale mafunde ace acita gabvigabvi, alephera; ngakhale akokoma, sangathe kupitirirapo.

23. Koma anthu awa ali ndi mtima woukirana ndi wopikisana; anapanduka nacoka.

24. Ndipo sanena m'mtima mwao, Tiopetu Yehova Mulungu wathu wopatsa mvula yoyamba ndi yamasika, m'nyengo yace; atisungira ife masabata olamulidwa a masika.

25. Mphulupulu zanu zacotsa zimenezi, ndi zocimwa zanu zakukanitsani inu zinthu zabwino.

26. Pakuti mwa anthu anga aoneka anthu oipa; adikira monga akucha misampha; acha khwekhwe, agwira anthu.

27. Monga cikwere codzala ndi mbalame, comweco nyumba zao zadzala ndi cinyengo; cifukwa cace akula, alemera,

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 5