2. Yehova Mulungu wa Israyeli atero kwa inu, Baruki:
3. Munati, Kalanga ine tsopano! pakuti Yehova waonjezera cisoni pa zowawa zanga; ndalema ndi kubuula kwanga, sindipeza kupuma,
4. Uzitero naye, Yehova atero: Taonani, cimene ndamanga ndidzapasula, ndi cimene ndaoka ndidzazula; ndidzatero m'dziko lonseli.
5. Kodi udzifunira wekha zinthu zazikuru? usazifune; pakuti, taona, ndidzatengera zoipa pa anthu onse, ati Yehova: koma moyo wako ndidzakupatsa iwe ngati cofunkha m'malo monse m'mene mupitamo.