Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 4:24-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Ndinaona mapiri, taona ananthunthumira; ndipo zitunda zonse zinagwedezeka.

25. Ndinaona, ndipo taona, panalibe munthu, ndi mbalame zonse zakumwamba zinathawa.

26. Ndinaona, ndipo taona, munda wazipatso unali cipululu, ndipo midzi yace yonse inapasuka pamaso pa Yehova, ndi pamaso pa mkwiyo wace woopsya.

27. Pakuti Yehova atero, Dziko lonse lidzakhala bwinja koma sindidzatsirizitsa.

28. Cifukwa cimeneco dziko lidzalira maliro, ndipo kumwamba kudzada; cifukwa ndanena, ndatsimikiza mtima, sindinatembenuka, sindidzabwerera pamenepo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 4