Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 39:7-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo anakolowola maso a Zedekiya, nammanga m'zigologolo, kunka naye ku Babulo.

8. Ndipo Akasidi anatentha ndi moto nyumba ya mfumu, ndi nyumba za anthu, nagumula malinga a Yerusalemu.

9. Ndipo Nebuzaradani kapitao wa alonda anatenga anthu otsalira m'mudzi, ndi othawa omwe, opandukira, ndi kumtsata ndi anthu otsalira nanka nao am'nsinga ku Babulo.

10. Koma aumphawi a anthu, amene analibe kanthu, Nebuzaradani kapitao wa alonda anawasiya m'dziko la Yuda, nawapatsa mipesa ndi minda nthawi yomweyo.

11. Ndipo Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo anamuuza Nebuzaradani kapitao wa alonda, za Yeremiya, kuti,

12. Umtenge, numyang'anire bwino, usamsautse, koma umcitire monga iye adzanena nawe.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 39