Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 39:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo anakolowola maso a Zedekiya, nammanga m'zigologolo, kunka naye ku Babulo.

8. Ndipo Akasidi anatentha ndi moto nyumba ya mfumu, ndi nyumba za anthu, nagumula malinga a Yerusalemu.

9. Ndipo Nebuzaradani kapitao wa alonda anatenga anthu otsalira m'mudzi, ndi othawa omwe, opandukira, ndi kumtsata ndi anthu otsalira nanka nao am'nsinga ku Babulo.

10. Koma aumphawi a anthu, amene analibe kanthu, Nebuzaradani kapitao wa alonda anawasiya m'dziko la Yuda, nawapatsa mipesa ndi minda nthawi yomweyo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 39