Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 38:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo anamkweza Yeremiya ndi zingwe, namturutsa m'dzenjemo; ndipo Yeremiya anakhalabe m'bwalo la kaidi.

14. Ndipo mfumu Zedekiya anatuma, natntenga Yeremiya mneneri nalowa naye m'khomo lacitatu la nyumba ya Yehova; ndipo mfumu inati kwa Yeremiya, Ndidzakufunsa iwe kanthu; usandibisire ine kanthu.

15. Ndipo Yeremiya anati kwa Zedekiya, Ndikakufotokozerani, kodi simudzandipha ine? ndipo ndikakupangirani, simudzandimveta ine.

16. Ndipo Zedekiya analumbira m'tseri kwa Yeremiya, kuti, Pali Yehova, amene anatilengera ife moyo uno, sindidzakupha iwe sindidzakupereka iwe m'manja mwa anthu awa amene afuna moyo wako.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 38