Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 37:3-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo Zedekiya mfumu anatuma Yehukali mwana wa Selemiya, ndi Zefaniya mwana wa Maseya wansembe, kwa Yeremiya mneneri, kukanena, Mutipemphereretu kwa Yehova Mulungu wathu.

4. Ndipo Yeremiya analikuyendayenda mwa anthu; cifukwa asanamuike iye m'nyumba yandende.

5. Ndipo nkhondo ya Farao inaturuka m'Aigupto; ndipo pamene Akasidi omangira misasa Yerusalemu anamva mbiri yao, anacoka ku Yerusalemu.

6. Ndipo mau a Yehova anadza kwa Yeremiya mneneri, kuti,

7. Atero Yehova, Mulungu wa Israyeli: Muzitero kwa mfumu ya Yuda, imene inakutumani inu kwa Ine kuti mundifunse Ine: Taonani, nkhondo ya Farao, yakuturukira kudzathandiza inu, idzabwerera ku Aigupto ku dziko lao.

8. Ndipo Akasidi adzabweranso, nadzamenyana ndi mudzi uwu; ndipo adzaulanda, nadzautentha ndi moto.

9. Yehova atero: Musadzinyenge, kuti, Akasidi adzaticokera ndithu; pakuti sadzacoka.

10. Pakuti ngakhale mukadakantha nkhondo yonse ya Akasidi akumenyana, nanu, ngakhale akadatsala olasidwa okha okha mwa iwo, koma iwowa akadauka yense m'hema wace ndi kutentha mudzi uwu ndi moto.

11. Ndipo panali pamene nkhondo ya Akasidi inacoka ku Yerusalemu cifukwa ca nkhondo ya Farao,

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 37