Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 35:17-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Cifukwa cace atero Yehova, Mulungu wa makamu, Mulungu wa Israyeli: Taonani, ndidzafikitsa pa Yuda ndi pa onse okhala m'Yerusalemu coipa conseco ndawanenera iwo; cifukwa ndanena ndi iwo, koma sanamve; ndaitana, koma iwo sanandibvomera.

18. Ndipo Yeremiya anati kwa nyumba ya Arekabu, Atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli: Cifukwa mwamvera lamulo la Yonadabu kholo lanu, ndi kusunga zonse anakulangizani inu, ndi kucita monga mwa zonse anakuuzani inu;

19. cifukwa cace atero Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli: Yonadabu mwana wa Rekabu sadzasowa munthu wakuima pamaso panga kumuyaya.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 35