Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 33:1-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo mau a Yehova anadza kwa Yeremiya nthawi yaciwiri, pamene iye anali citsekedwere m'bwalo la kaidi, kuti,

2. Atero Yehova wocita zace, Yehova wolenga zace kuti azikhazikitse; dzina lace ndi Yehova:

3. Undiitane Ine, ndipo Ine ndidzakuyankha iwe, ndipo ndidzakusonyeza iwe zazikuru, ndi zolakika, zimene suzidziwa.

4. Pakuti atero Yehova, Mulungu wa Israyeli, za nyumba za mudzi uno, ndi za nyumba za mafumu a Yuda'zi, zinagwetsedwa ziwacinjirizire mitumbira, ndi lupanga:

5. Adza kumenyana ndi Akasidi, koma adzangozidzaza ndi mitembo ya anthu, amene ndawapha m'mkwiyo wanga ndi mu ukali wanga, amene ndabisira mudzi uno nkhope yanga cifukwa ca zoipa zao zonse.

6. Taonani, ndidzautengera moyo ndi kuuciritsa, ndi kuwaciritsa; ndipo ndidzawaululira iwo kucuruka kwa mtendere ndi zoona.

7. Ndipo ndidzabweza undende wa Yuda ndi wa Israyeli, ndipo ndidzamangitsa mudzi wao, monga poyamba paja,

8. Ndipo ndidzawayeretsa kucotsa mphulupulu yao, imene anandicimwira Ine; ndipo ndidzakhululukira mphulupulu zao zimene anandicimwira, nandilakwira Ine.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 33