Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 32:6-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo Yeremiya anati, Mau a Yehova anadza kwa ine, kuti,

7. Taonani, Hanameli mwana wa Salumu mbale wa atate wako adzadza kwa iwe, kuti, Ugule munda wanga uli ku Anatoti; pakuti mphamvu yakuombola ndi yako kuugula.

8. Ndipo Hanameli mwana wa mbale wa atate wanga anadza kwa ine m'bwalo la kaidi monga mwa mau a Yehova, nati kwa ine, Gulatu munda wanga, wa ku Anatoti, m'dziko la Benjamini; pakuti mphamvu yakulowa ndi yakuombola ndi yako; udzigulire wekha. Pamenepo ndinadziwa kuti awa ndi mau a Yehova.

9. Ndipo ndinagula mundawo wa ku Anatoti kwa Hanameli mwana wa cibale wa atate wanga, ndimyesera ndalama, masekele khumi ndi asanu ndi awiri a siliva.

10. Ndipo ndinalemba cikalataco, ndicisindikiza, ndiitana mboni zambiri, ndiyesa ndalama m'miyeso.

11. Ndipo ndinatenga kalata wogulira, wina wosindikizidwa, monga mwa lamulo ndi mwambo, ndi wina wobvundukuka;

12. ndipo ndinapereka kalata wogulirayo kwa Baruki mwana wa Neriya, mwana wa Maseya, pamaso pa Hanameli mwana wa mbale wa atate wanga, ndi pamaso pa mboni zimene zinalemba pa kalata wogulirayo, pamaso pa Ayuda onse okhala m'bwalo la kaidi.

13. Ndipo ndinauza Baruki pamaso pao, kuti,

14. Yehova wa makamu, Mulungu wa Israyeli atero; Tenga akalata awa, kalata uyu wogulira, wosindikizidwa, ndi kalata uyu wobvundukuka, nuwaike m'mbiya yadothi; kuti akhale masiku ambiri.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 32