Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 31:37-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

37. Atero Yehova, Ngati ukhoza kuyesa thambo la kumwamba, ndi kusanthula pansi maziko a dziko, pamenepo ndidzacotsa mbeu zonse za Israyeli cifukwa ca zonse anazicita, ati Yehova.

38. Taonani, masiku adza, ati Yehova, amene mudziwu udzamangidwira Yehova kuyambira pa nsanja ya Hananeli kufikira ku cipata ca kungondya.

39. Ndipo cingwe coyesera cidzaturukanso kulunjika ku citunda ca Garebi, ndipo cidzazungulira kunka ku Goa.

40. Ndipo cigwa conse ca mitembo, ndi ca phulusa, ndi minda yonse: kufikira ku mtsinje wa Kidroni, kufikira kungondya kwa cipata ca akavalo kuloza kum'mawa, ponsepo padzapatulikira Yehova; sipadzazulidwa, sipadzagwetsedwa konse ku nthawi zamuyaya.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 31