1. Nthawi yomweyo, ati Yehova, ndidzakhala Mulungu wa mabanja onse a Israyeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
2. Atero Yehova, Anthu opulumuka m'lupanga anapeza cisomo m'cipululu; Israyeli, muja anakapuma.
3. Yehova anaonekera kwa ine kale, ndi kuti, Inde, ndakukonda iwe ndi cikondi cosatha; cifukwa cace ndakukoka iwe ndi kukukomera mtima.
4. Ndidzamangitsanso mudzi wako, ndipo udzamangidwa, iwe namwali wa Israyeli; udzakometsedwanso ndi mangaka, ndipo udzaturukira masewero a iwo akukondwerera.
5. Ndiponso udzalima minda ya mphesa pa mapiri a Samariya; akunka adzanka, nadzayesa zipatso zace zosapatulidwa.
6. Pakuti lidzafika tsiku, limene alonda a pa mapiri a Efraimu adzapfuula, Ukani inu, tikwere ku Ziyoni kwa Yehova Mulungu wathu.
7. Pakuti Yehova atero, Yimbirirani Yakobo ndi kukondwa, pfuulirani mtundu woposawo; lalikirani, yamikirani, ndi kuti, Yehova, mupulumutse anthu anu, ndi otsala a Israyeli,
8. Taonani, ndidzatenga iwo ku dziko la kumpoto, ndidzasonkhanitsa iwo ku malekezero a dziko lapansi, pamodzi ndi osaona ndi opunduka mwendo, mkazi amene ali ndi pakati ndi mkazi alinkubala pamodzi; khamu lalikuru lidzabwera kuno.