Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 30:19-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo padzaturuka pa izo mayamikiro ndi mau a iwo okondwerera; ndipo ndidzacurukitsa iwo, sadzakhala owerengeka; ndidzawacitiranso ulemu, sadzacepa.

20. Ana aonso adzakhala monga kale, ndipo msonkhano wao udzakhazikika pamaso panga, ndipo ndidzalanga onse amene akupsinja iwo.

21. Ndipo mkuru wao adzakhala mwa iwo, ndi wolamulira wao adzaturuka pakati pao; ndipo ndidzamyandikitsa iye, ndipo adzayandikira kwa Ine, pakuti iye wolimba mtima kuyandikira kwa Ine ndani? ati Yehova.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 30