Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 3:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Amati, Ngati mwamuna acotsa mkazi wace, ndipo amcokera iye, nakhala mkazi wa wina, kodi adzabweranso kwa mkaziyo? dzikolo kodi silidzaipitsidwa? Koma iwe wacita dama ndi mabwenzi ambiri; koma bweranso kwa Ine, ati Yehova.

2. Kwezera maso ako ku mapiri oti se, nuone: sanagona ndi iwe kuti? Panjira wakhalira iwo, monga M-arabu m'cipululu; ndipo waipitsa dziko ndi zigololo zako, ndi zoipa zako.

3. Ndipo mvula yakanidwa, ndipo panalibe mvula ya masika; ndipo unali ndi nkhope ya mkazi wadama, unakana manyazi.

4. Kodi kuyambira tsopano sudzapfuulira kwa Ine, Atate wanga, wotsogolera ubwana wanga ndinu?

5. Kodi adzasunga mkwiyo wace ku nthawi zonse? Kodi adzakudikira mpaka cimariziro? Taona, wanena ndi kucita zoipa monga unatero.

6. Ndipo Yehova anati kwa ine masiku a Yosiya mfumu, Kodi waona cimene wacicita Israyeli, wobwerera m'mbuyo? Wakwera pa mapiri atari onse, ndi patsinde pa mitengo yaiwisi yonse, ndi kucita dama pamenepo.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 3