Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 28:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Koma mumvetu mau awa amene ndinena m'makutu anu, ndi m'makutu a anthu onse:

8. Aneneri amene analipo kale ndisanakhale ine, nimusanakhale inu, ananenera maiko ambiri, ndi maufumu akuru, za nkhondo, ndi za coipa, ndi za caola.

9. Mneneri amene anenera za mtendere, pamene mau a mneneri adzacitidwa, pamenepo mneneri adzadziwika, kuti Yehova anamtuma ndithu.

10. Pamenepo Hananiya anacotsa gori pa khosi la Yeremiya, nalityola.

11. Ndipo Hananiya ananena pamaso pa anthu onse, kuti, Yehova atero: Comweco ndidzatyola gori la Nebukadinezara mfumu ya Babulo zisanapite zaka ziwiri zamphumphu kulicotsa pa khosi la amitundu onse. Ndipo Yeremiya mneneri anacoka.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 28