Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 25:2-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. amene Yeremiya ananena kwa anthu onse a Yuda, ndi onse okhala m'Yerusalemu, kuti:

3. Kuyambira caka cakhumi ndi citatu ca Yosiya mwana wace wa Amoni, mfumu ya Yuda, kufikira lero lomwe, zakazi makumi awiri ndi zitatu, mau a Yehova anafika kwa ine, ndipo ndanena kwa inu, pouka mamawa ndi kunona; koma simunamvera.

4. Ndipo Yehova watuma kwa inu atumiki ace onse ndiwo aneneri, pouka mamawa ndi kuwatuma; koma simunamvera, simunachera khutu lanu kuti mumve;

5. ndi kuti, Mubwerere tsopano nonsenu, yense kuleka njira yace yoipa, ndi zoipa za nchito zanu, ndi kukhala m'dziko limene Yehova anapatsa inu ndi makolo anu, kuyambira kale kufikira muyaya;

6. musatsate milungu yina kuitumikira, ndi kuigwadira, musautse mkwiyo wanga ndi nchito ya manja anu; ndingacitire inu coipa.

7. Koma simunandimvera Ine, ati Yehova; kuti muutse mkwiyo wanga ndi nchito ya manja anu ndi kuonapo coipa inu.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 25