Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 23:3-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo ndidzasonkhanitsa zotsala za zoweta zanga za m'maiko onse m'mene ndinazipitikitsiramo, ndipo ndidzazitengeranso ku makola ao; ndipo zidzabalana ndi kucuruka.

4. Ndipo ndidzaziikira abusa amene adzazidyetsa; sadzaopanso, kapena kutenga nkhawa, sipadzasowa mmodzi yense, ati Yehova.

5. Taonani, masiku alinkudza, ati Yehova, ndidzamuukitsira Davide Mphukira wolungama, ndipo Iye adzakhala Mfumu, adzacita mwanzeru, nadzacita ciweruzo ndi cilungamo m'dziko lino.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 23