Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 23:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Tsoka abusa amene athetsa nabalalitsa nkhosa za busa langa! ati Yehova.

2. Cifukwa cace atero Yehova, Mulungu wa Israyeli, ponenera abusa amene adyetsa anthu anga: Mwabalalitsa zoweta zanga, ndi kuzipitikitsa, ndipo simunazizonda; taonani, ndidzakusenzani inu kuipa kwa nchito zanu, ati Yehova.

3. Ndipo ndidzasonkhanitsa zotsala za zoweta zanga za m'maiko onse m'mene ndinazipitikitsiramo, ndipo ndidzazitengeranso ku makola ao; ndipo zidzabalana ndi kucuruka.

4. Ndipo ndidzaziikira abusa amene adzazidyetsa; sadzaopanso, kapena kutenga nkhawa, sipadzasowa mmodzi yense, ati Yehova.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 23