Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 17:10-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ine Yehova ndisanthula mtima, ndiyesa imso, kuti ndimpatse munthu yense monga mwa njira zace, monga zipatso za nchito zace.

11. Monga nkhwali iumatira pa mazira amene sinaikira, momwemo iye amene asonkhanitsa cuma, koma mosalungama; pakati pa masiku ace cidzamsiya iye, ndipo pa citsirizo adzakhala wopusa.

12. Malo opatulika athu ndiwo mpando wacifumu wa ulemerero, wokhazikika pamsanje ciyambire.

13. Inu Yehova, ciyembekezo ca Israyeli, onse amene akukusiyani Inu adzakhala ndi manyazi; onse ondicokera Ine adzalembedwa m'dothi, cifukwa asiya Yehova, kasupe wa madzi amoyo.

14. Mundiciritse ine, Yehova, ndipo ndidzaciritsidwa; mundipulumutse ine, ndipo ndidzapulumutsidwa; pakuti cilemekezo canga ndinu.

15. Taonani, ati kwa ine, Mau a Yehova ali kuti? adze tsopano.

16. Koma ine, pokhala mbusa sindinafulumira kucokerako kuti ndikutsateni Inu; sindinakhumba tsiku la tsoka; Inu mudziwa, cimene cinaturuka pa milomo yanga cinali pamaso panu.

17. Musakhale wondiopsetsa ine; ndinu pothawira panga tsiku la coipa.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 17