Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 12:4-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Dziko lidzalira masiku angati, nilifota therere la minda yonse? cifukwa ca zoipa za iwo okhalamo, zithedwa zinyama, ndi mbalame; pakuti iwo anati, Iye sadzaona citsiriziro cathu.

5. Ngati wathamanga pamodzi ndi oyenda pansi, ndipo iwo anakulemetsa iwe, udzayesana nao akavalo bwanji? ndipo ngakhale ukhazikika m'dziko lamtendere, udzacita ciani m'kudzikuza kwa Yordano?

6. Pakuti ngakhale abale ako, ndi nyumba ya atate wako, ngakhale iwo anakunyenga iwe; ngakhale anakupfuulira iwe; usamvere iwo, ngakhale anena nawe mau abwino.

7. Ndacokaku nyumba yanga, ndasiya colowa canga; ndapereka wokondedwa wa mtima wanga m'dzanja la adani.

8. Colowa canga candisandukira mkango wa m'nkhalango; anatsutsana nane ndi mau ace; cifukwa cace ndinamuda.

9. Colowa canga ciri kwa ine ngati mbalame yamawala-mawala yolusa? kodi mbalame zolusa zimzinga ndi kudana naye? mukani, musonkhanitse zirombo za m'thengo, mudze nazo zidye.

10. Abusa ambiri aononga munda wanga wamphesa, apondereza gawo langa, pondikondweretsa apayesa cipululu copanda kanthu.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 12