Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 10:22-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

22. Mbiri yamveka, taonani ikudza, ndi phokoso lalikuru lituruka m'dziko la kumpoto, likacititse midzi ya Yuda bwinja, ndi mbuto ya nkhandwe.

23. Inu Yehova, ndidziwa kuti njira ya munthu siri mwa iye mwini; sikuli kwa munthu woyenda kulongosola mapazi ace.

24. Yehova, mundilangize, koma ndi ciweruzo; si m'mkwiyo wanu, mungandithe psiti.

25. Tsanulirani ukali wanu pa amitundu osakudziwani Inu, ndi pa mabanja osaitana dzina lanu; pakuti anadya Yakobo, inde, anamudya namutha, napasula mokhalamo mwace.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 10