Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Rute 2:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo mpongozi wace ananena naye, Unakatola kuti khunkha lero? ndi nchito udaigwira kuti? Adalitsike iye amene anakusamalira. Ndipo anamfotokozera mpongozi wace munthu amene anakagwirako nchito, nati, Dzina lace la munthuyo ndinakagwirako nchito lero ndiye Boazi.

20. Nati Naomi kwa mpongozi wace, Yehova amdalitse amene sanaleka kuwacitira zokoma amoyo, ndi akufa. Ndipo Naomi ananena baye, Munthuyu ndiye mbale wathu, ndiye mmodzi wa iwo otiombolera colowa.

21. Ndipo Rute Mmoabu anati, Ananenanso nane ndithu, Uwaumirire anyamata anga, mpaka atatha kuceka zanga zonse za m'minda.

22. Nati Naomi kwa Rute mpongozi wace, Ncabwino, mwana wanga, kuti uzituruka nao adzakazi ace, ndi kuti asakukomane m'munda wina uti wonse.

Werengani mutu wathunthu Rute 2