Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Oweruza 9:49-55 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

49. Ndi anthu onse anadulanso yense nthambi yace, natsata Abimeleki, naziika pangaka, natentha nazo ngakayo ndi moto; motero anthu onse a nsanja ya ku Sekemu anafanso, amuna ndi akazi ngati cikwi cimodzi.

50. Pamenepo Abimeleki anamuka ku Tebetsi, naumangira Tebetsi misasa, naulanda.

51. Koma m'mudzimo munali nsanja yolimba nathawira kumeneko amuna ndi akazi onse, ndi eni ace onse a mudziwo, nadzitsekereza m'mwemo, nakwera patsindwi pa nsanja.

52. Ndipo Abimeleki anafika kunsania, nalimbana nayo nkhondo, nayandikira kukhomo kwa nsanja, aitenthe ndi moto.

53. Ndipo mkazi wina anaponya mwana wa mphero pamutu pa Abimeleki, naphwanya bade lace.

54. Pamenepo anaitana msanga mnyamata wace wosenza zida zace, nanena naye, Solola lupanga lako nundiphe, angamanenere anthu, ndi kuti, Anamupha ndi mkazi. Nampyoza mnyamata wace, nafa iye.

55. Pamene amuna a Israyeli anaona kuti adafa Abimeleki anamuka yense kumalo kwace.

Werengani mutu wathunthu Oweruza 9