27. Koma Manase sanaingitsa a ku Betiseani ndi midzi yace kapena a Taanaki ndi midzi yace, kapena nzika za ku Dori ndi midzi yace, kapena nzika za ku Ibleamu ndi midzi yace, kapena nzika za ku Megido ndi midzi yace; koma Akanani anakhumba kukhala m'dziko muja.
28. Ndipo kunali, atakula mphamvu Israyeli, anasonkhetsa Akanani, osawaingitsa onse.
29. Ndipo Efraimu sanaingitsa Akanani okhala m'Gezeri; koma Akanani anakhala m'Gezeri pakati pao,
30. Zebuloni sanaingitsa nzika za ku Kitroni, kapena nzika za ku Nahaloli; koma Akanaru anakhala pakati pao, nawasonkhera.
31. Aseri sanaingitsa nzika za ku Ako, kapena nzika za ku Sidoni, kapena a Akalabu, kapena a Akisibu, kapena a Heliba, kapena a Afiki, kapena a Rehobo;
32. koma Aseri anakhala pakati pa Akanani nzika za kudziko; pakuti sanawaingitsa.
33. Nafitali sanaingitsa nzika za ku Beti-semesi, kapena nzika za ku Beri-anati; koma anakhala pakati pa Akanani, nzika za kudziko; koma nzika za ku Beti-semesi, ndi a ku Beti-anati zinawasonkhera.
34. Ndipo Aamori anakankha ana a Dani akhale kumapiri pakuti sanawalola atsikire kucigwa;
35. Aamori anakhumbanso kukhala ku phiri la Heresi, ku Ajaloni, ndi ku Saalibimu; koma dzanja la a m'nyumba ya Yosefe linawalaka, nakhala iwo akupereka msonkho.
36. Ndipo malire a Aamori anayambira pokwerera pa Akrabimu, pathanthwe, ndi pokwererapo.