24. Ndipo alonda anaona munthu alikuturuka m'mudzi, nanena naye, Utionetsetu nolowera m'mudzi, ndipo tidzakucitira cifundo.
25. Nawaonetsa polowera m'mudzi iye, naukantha mudzi iwowa ndi lupanga lakuthwa; koma analola munthuyo ndi banja lace lonse amuke.
26. Ndipo munthuyo anamuka ku dziko la Ahiti, namanga mudzi, naucha dzina lace Luzi; ndilo dzina lace mpaka lero lino.
27. Koma Manase sanaingitsa a ku Betiseani ndi midzi yace kapena a Taanaki ndi midzi yace, kapena nzika za ku Dori ndi midzi yace, kapena nzika za ku Ibleamu ndi midzi yace, kapena nzika za ku Megido ndi midzi yace; koma Akanani anakhumba kukhala m'dziko muja.
28. Ndipo kunali, atakula mphamvu Israyeli, anasonkhetsa Akanani, osawaingitsa onse.
29. Ndipo Efraimu sanaingitsa Akanani okhala m'Gezeri; koma Akanani anakhala m'Gezeri pakati pao,
30. Zebuloni sanaingitsa nzika za ku Kitroni, kapena nzika za ku Nahaloli; koma Akanaru anakhala pakati pao, nawasonkhera.
31. Aseri sanaingitsa nzika za ku Ako, kapena nzika za ku Sidoni, kapena a Akalabu, kapena a Akisibu, kapena a Heliba, kapena a Afiki, kapena a Rehobo;
32. koma Aseri anakhala pakati pa Akanani nzika za kudziko; pakuti sanawaingitsa.