12. Ana a maso ace akunga nkhunda pambali pa mitsinje ya madzi;Otsukidwa ndi mkaka, okhala pa mitsinje yodzala.
13. Masaya ace akunga citipula cabzyalamo ndiwo,Ngati mitumbira yoyangapo masamba onunkhira:Milomo yace ikunga akakombo, pakukhapo madzi a nipa.
14. Manja ace akunga zing'anda zagolidi zoikamo zonyezimira zoti biriwiri:Thupi lace likunga copanga ca minyanga colemberapo masafiro.
15. Miyendo yace ikunga zoimiritsa za mwala wonyezimira,Zogwirika m'kamwa mwa golidi:Maonekedwe ace akunga Lebano, okometsetsa ngati mikungudza.
16. M'kamwa mwace muli mokoma: inde, ndiye wokondweretsa ndithu.Ameneyu ndi wokondedwa wanga, ameneyu ndi bwenzi langa,Ana akazi inu a ku Yerusalemu.