Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Nyimbo 2:5-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Mundilimbikitse ndi mphesa zouma, munditonthoze mtima ndi maula,Pakuti ndadwala ndi cikondi.

6. Dzanja lace lamanzere anditsamiritse kumutu,Dzanja lace lamanja ndi kundifungatira.

7. Ndikulumbirirani, ana akazi inu a ku Yerusalemu,Pali mphoyo, ndi nswala za kuthengo,Kuti musautse, ngakhale kugalamutsa cikondi,Mpaka cikafuna mwini.

8. Mau a wokondedwa wanga mnyamatayo! Taona, adza,Alikulumpha pamapiri, alikujidimuka pazitunda.

9. Wokondedwa wanga akunga mphoyo, pena mwana wa mbawala:Taona, aima patseri pa khoma pathu,Apenyera pazenera, Nasuzumira pamade.

10. Wokondedwa wanga analankhula, nati kwa ine,Tauka, bwenzi langa, wokongola wanga, tiye.

11. Pakuti, taona, cisanu catha,Mvula yapita yaleka;

12. Maluwa aoneka pansi;Nthawi yoyimba mbalame yafika,Mau a njiwa namveka m'dziko lathu;

13. Mkuyu uchetsa nkhuyu zace zosakhwima,Mipesa niphuka,Inunkhira bwino.Tauka, bwenzi langa, wokongola wangawe, tiyetu.

14. Nkhunda yangawe, yokhala m'ming'alu ya thanthwe, mobisika motsetsereka,Ndipenye nkhope yako, ndimve manako;Pakuti mau ako ngokoma, nkhope yako ndi kukongola.

15. Mutigwirire ankhandwe, ngakhale ang'ono, amene akuononga minda yamipesa;Pakuti m'minda yathu yamipesa muphuka biriwiri.

16. Wokondedwa wanga ndi wa ine, ine ndine wace:Aweta zace pakati pa akakombo,

Werengani mutu wathunthu Nyimbo 2