19. Ndipo pakukhalitsa mtambo masiku ambiri pamwamba pa kacisi, pamenepo ana a Israyeli anasunga udikiro wa Yehova osayenda ulendo.
20. Ndipo pokhala mtambo pamwamba pa kacisi masiku pang'ono; pamenepo anakhala m'cigono monga awauza Yehova, nayendanso ulendo monga anauza Yehova.
21. Koma mtambo ukakhala kuyambira madzulo kufikira m'mawa; pokwera mtambo m'mawa, ayenda ulendo; ngakhale msana ngakhale usiku, pokwera mtambo, ayenda ulendo.
22. Ngakhale masiku awiri, kapena mwezi, kapena masiku ambiri, pokhalitsa mtambo pamwamba pa kacisi ndi kukhalapo, ana a Israyeli anakhala m'cigono, osayenda ulendo; koma pakukwera uwu, anayenda ulendo.
23. Powauza Yehova amanga mahema, powauza Yehova ayenda ulendo; anasunga udikiro wa Yehova powauza Yehova mwa dzanja la Mose.