Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 5:8-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Koma munthuyo akapanda kukhala nayo nkhoswe imene akaibwezere coparamulaco, coparamula acibwezera Yehovaco cikhale ca wansembe; pamodzi ndi nkhosa yamphongo ya cotetezerapo, imene amcitire nayo comtetezera.

9. Ndipo nsembe zokweza zonse za zinthu zopatulika za ana a Israyeli, zimene abwera nazo kwa wansembe zisanduka zace.

10. Zopatulika za munthu ali yense ndi zace: ziti zonse munthu ali yense akapatsa wansembe, zasanduka zace.

11. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

12. Nena ndi ana a Israyeli, nuti nao, Mkazi wa mwini akapatukira mwamuna wace, nakamcitira mosakhulupirika,

13. ndi munthu akagona naye, koma kumbisikira maso a mwamuna wace, ndikumng'unira; nadetsedwa mkaziyo, koma palibe mboni yomtsutsa, kapena sanamgwira alimkucita;

14. ndipo ukamgwira mwamuna mtima wansanje, kuti acitire nsanje mkazi wace, popeza wadetsedwa; kapena ukamgwira mtima wansanje, kuti amcitire mkazi wace nsanje angakhale sanadetsedwa;

15. pamenepo mwamunayo azidza naye mkazi wace kwa wansembe, nadze naco copereka cace, limodzi la magawo khumi la efa wa ufa wabarele; asathirepo mafuta, kapena kuikapo libano; popeza ndiyo nsembe yaufa yansanje, nsembe yaufa yacikumbutso, yakukumbutsa mphulupulu.

16. Ndipo wansembe abwere naye, namuike pamaso pa Yehova;

17. natenge madzi opatulika m'mbale yadothi wansembeyo, natengeko pfumbi liri pansi m'kacisi, wansembeyo nalithire m'madzimo.

18. Pamenepo wansembeyo aike mkaziyo pamaso pa Mulungu, nabvula mutu wa mkaziyo, naike nsembe yaufa yacikumbutso m'manja mwace, ndiyo nsembe yaufa yansanje; ndipo m'manja mwace mwa wansembe muzikhala madzi owawa akudzetsa temberero.

19. Ndipo wansembe amlumbiritse, nanene kwa mkazi, Ngati sanagona nawe munthu mmodzi yense, ngati sunapatukira kucidetso, pokhala ndiwe wa mwamuna wako, upulumuke ku madzi owawa awa akudzetsa temberero.

20. Koma iwe, ngati wapatukira mwamuna wako, ngati wadetsedwa, kuti wagona nawe munthu, wosati mwamuna wako;

21. pamenepo wansembe alumbiritse mkazi lumbiro lakutemberera, ndi wansembe anene kwa mkazi, Yehova akuike ukhale temberero ndi lumbiro pakati pa anthu a mtundu wako, pakuondetsa Yehova m'cuuno mwako, ndi kukutupitsa mbulu;

22. ndipo madzi awa akudzetsa temberero adzalowa m'matumbo mwako, nadzakutupitsa mbulu ndi kuondetsa m'cuuno mwako; ndipo mkaziyo aziti, Amen, Amen.

Werengani mutu wathunthu Numeri 5