Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 4:8-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo ayale pa izi nsaru yofiira, ndi kuliphimba ndi cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kupisako mphiko zace.

9. Ndipo atenge nsaru yamadzi, ndi kuphimba coikapo nyali younikira, ndi nyali zace, ndi mbano zace, ndi zaolera zace, ndi zotengera zace zonse za mafuta zogwira nazo nchito yace.

10. Ndipo acimange ndi cipangizo zace zonse m'cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kuziika pa conyamulira.

11. Ndipo pa guwa la nsembe lagolidi aziyala nsaru yamadzi, naliphimbe ndi cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kupisako mphiko zace.

12. Natenge zipangizo zace zonse za utumiki, zimene atumikira nazo m'malo opatulika, nazimange m'nsaru yamadzi, ndi kuziphimba ndi cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kuziika paconyamulira.

13. Ndipo azicotsa mapulusa pa guwa la nsembe, ndi kuyala pa ilo nsaru yofiirira.

14. Naikepo zipangizo zace zonse, zimene atumikira nazo pamenepo, mbale za zofukiza, mitungo, ndi zaolera, ndi mbale zowazira, zipangizo zonse za guwa la nsembe; nayalepo cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kupisako mphiko zace.

15. Atatha Aroni ndi ana ace amuna kuphimba malo opatulika, ndi zipangizo zace zonse za malo opatulika, pofuna kumuka am'cigono; atatero, ana a Kohati adze kuzinyamula; koma asakhudze zopatulikazo, kuti angafe. Zinthu izi ndizo akatundu a ana a Kohati m'cihema cokomanako.

Werengani mutu wathunthu Numeri 4