Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 4:10-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo acimange ndi cipangizo zace zonse m'cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kuziika pa conyamulira.

11. Ndipo pa guwa la nsembe lagolidi aziyala nsaru yamadzi, naliphimbe ndi cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kupisako mphiko zace.

12. Natenge zipangizo zace zonse za utumiki, zimene atumikira nazo m'malo opatulika, nazimange m'nsaru yamadzi, ndi kuziphimba ndi cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kuziika paconyamulira.

13. Ndipo azicotsa mapulusa pa guwa la nsembe, ndi kuyala pa ilo nsaru yofiirira.

14. Naikepo zipangizo zace zonse, zimene atumikira nazo pamenepo, mbale za zofukiza, mitungo, ndi zaolera, ndi mbale zowazira, zipangizo zonse za guwa la nsembe; nayalepo cophimba ca zikopa za akatumbu, ndi kupisako mphiko zace.

15. Atatha Aroni ndi ana ace amuna kuphimba malo opatulika, ndi zipangizo zace zonse za malo opatulika, pofuna kumuka am'cigono; atatero, ana a Kohati adze kuzinyamula; koma asakhudze zopatulikazo, kuti angafe. Zinthu izi ndizo akatundu a ana a Kohati m'cihema cokomanako.

16. Ndipo zoyang'anira Eleazara, mwana wa Aroni wansembe, ndizo mafuta a nyaliyo, ndi cofukiza ca pfungo lokoma, ndi nsembe yaufa kosalekeza, ndi mafuta odzoza, udikiro wa kacisi wonse, ndi zonse ziri m'mwemo, malo opatulika, ndi zipangizo zace.

17. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, Dati,

18. Musamasadza pfuko la mabanja a Kohati kuwacotsa pakati pa Alevi;

19. koma muzitero nao kuti akhale ndi moyo, osafa ai, poyandikiza iwo zopatulikitsazo; Aroni ndi ana ace amuna alowe, namuikire munthu yense nchito yace ndi katundu wace.

20. Koma asalowe kukaona zopatulikazo pozikulunga, kuti angafe.

21. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

22. Werenganso ana a Gerisoni, monga mwa nyumba za makolo ao, monga mwa mabanja ao.

23. Uwawerenge kuyambira a zaka makumi atatu ndi mphambu, kufikira a zaka makumi asanu; onse akulowa kutumikira utumikiwo, kucita nchitoyi m'cihema cokomanako.

24. Nchito ya mabanja a Agerisoni, pogwira nchito ndi kusenza katundu ndi iyi;

Werengani mutu wathunthu Numeri 4