Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 31:47-54 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

47. mwa gawolo la ana a Israyeli Mose anatenga munthu mmodzi mwa makumi asanu, ndi zoweta momwemo, nazipereka kwa Alevi, akusunga udikiro wa kacisi wa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.

48. Pamenepo akazembe a pa ankhondo zikwi, atsogoleri a zikwi, ndi atsogoleri a mazana, anayandikiza kwa Mose;

49. nati kwa Mose, Atumiki anu anawerenga ankhondo tinali nao, ndipo sanasowa munthu mmodzi wa ife.

50. Ndipo tabwera naco copereka ca Yehova, yense cimene anacipeza, zokometsera zagolidi, unyolo, zikwinjiri, mphete zosindikizira, nsapule, ndi mkanda, kucita cotetezera moyo wathu pamaso pa Yehova.

51. Ndipo Mose ndi Eleazara wansembe analandira golidiyo kwa iwowo, ndizo zokometsera zonse zokonzeka.

52. Ndipo golidi yense wa nsembe yokweza ya Yehova amene anapereka kwa Yehova, wofuma kwa atsogoleri a zikwi, ndi atsogoleri a mazana, ndiwo masekeli zikwi khumi ndi zisanu ndi cimodzi mphambu mazana asanu ndi awiri kudza makumi asanu.

53. Popeza wankhondo yense anadzifunkhira yekha.

54. Ndipo Mose ndi Eleazara wansembe analandira golidi kwa akuru a zikwi ndi a mazana, nalowa naye ku cihema cokomanako, cikumbutso ca ana a Israyeli pamaso pa Yehova.

Werengani mutu wathunthu Numeri 31