Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 31:29-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Uzitenge ku gawo lao, ndi kuzipereka kwa Eleazara wansembe, zikhale nsembe yokweza ya Yehova.

30. Ndipo ku gawo la ana a Israyeli utenge munthu mmodzi mwa anthu makumi asanu, mwa ng'ombe, mwa aburu, mwa nkhosa ndi mbuzi, mwa zoweta zonse, momwemo; nuzipereke kwa Alevi, akusunga udikiro wa kacisi wa Yehova.

31. Ndipo Mose ndi Eleazara wansembe anacita monga Yehova anamuuza Mose.

32. Ndipo zakunkhondo, zotsalira zofunkha zonse adazifunkha ankhondowa, ndizo nkhosa zikwi mazana asanu ndi limodzi mphambu zikwi makumi asanu ndi awiri kudza zisanu,

33. ndi ng'ombe zikwi makumi asanu ndi awiri mphambu ziwiri,

34. ndi aburu zikwi makumi asanu ndi limodzi mphambu cimodzi,

35. ndi anthu, ndiwo akazi osadziwa mwamuna mogona naye, onse pamodzi zikwi makumi atatu ndi ziwiri.

Werengani mutu wathunthu Numeri 31