Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 31:2-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Abwezereni cilango Amidyani cifukwa ca ana a Israyeli; utatero udzaitanidwa kumka kwa anthu a mtundu wako.

3. Ndipo Mose ananena ndi anthu, nati, Adzikonzere ena mwa inu zida za nkhondo, alimbane nao Amidyani, kuwabwezera Amidyani cilango ca Yehova.

4. Muwatume kunkhondo a pfuko limodzi, cikwi cimodzi, a pfuko limodzi cikwi cimodzi, atere mafuko onse a Israyeli.

5. Ndipo anapereka mwa zikwi za Israyeli, a pfuko limodzi cikwi cimodzi, anthu zikwi khumi ndi ziwiri okonzekeratu ndi zankhondo.

6. Ndipo Mose anawatuma a pfuko limodzi cikwi cimodzi, kunkhondo, iwowa ndi Pinehasi mwana wa Eleazara wansembe, kunkhondo, ndi zipangizo zopatulika, ndi malipenga oliza m'dzanja lace.

7. Ndipo anawathira nkhondo Amidyani, monga Yehova adamuuza Mose; nawapha amuna onse.

8. Ndipo anapha mafumu a Amidyani pamodzi ndi ophedwa ao ena; ndiwo Evi, ndi Rekamu, ndi Zuri, ndi Huri, ndi Reba, mafumu asanu a Amidyani; namupha Balamu mwana wa Beori ndi lupanga.

9. Ndipo ana a Israyeli anagwira akazi a Amidyani, ndi ana ang'ono, nafunkha ng'ombe zao zonse, ndi zoweta zao zonse, ndi cuma cao conse.

10. Ndipo anatentha ndi moto midzi yao yonse yokhalamo iwo, ndi zigono zao zonse.

11. Ndipo anapita nazo zofunkha zonse, ndi zakunkhondo zonse, ndizo anthu ndi nyama.

12. Ndipo anadza nao andende, ndi zakunkhondo, ndi zofunkha, kwa Mose, ndi kwa Eleazara wansembe, ndi kwa khamu la ana a Israyeli, kucigono, ku zidikha za Moabu, ziri ku Yordano pafupi pa Yeriko.

13. Ndipo Mose, ndi Eleazara wansembe, ndi akalonga onse a khamulo, anaturuka kukomana nao kunja kwa cigono.

14. Ndipo Mose anakwiya nao akazembe a nkhondoyi, atsogoleri a zikwi, atsogoleri a mazana, akufuma kunkhondo adaithira.

15. Ndipo Mose ananena nao, Kodi mwasunga ndi moyo akazi onse?

16. Taonani, awa analakwitsa ana a Israyeli pa Yehova nilica Peoricija, monga adawapangira Balamu; kotero kuti kunali mliri m'khamu la Yehova.

17. Ndipo tsono iphani amuna onse mwa anawo, iphaninso akazi onse akudziwa mwamuna mogona naye.

18. Koma ana akazi onse osadziwa mwamuna mogona naye, asungeru ndi moyo akhale anu.

19. Ndipo mukhale m'misasa kunja kwa cigono masiku asanu ndi awiri; ali yense adapha munthu, ndi ali yense wakukhudza wophedwa, mudziyeretse tsiku lacitatu ndi lacisanu ndi ciwiri, inu ndi andende anu.

20. Muyeretse zobvala zanu zonse, zipangizo zonse zacikopa, ndi zaomba zonse za ubweya wa mbuzi, ndi zipangizo zonse zamtengo.

21. Ndipo Eleazara wansembe ananena ndi ankhondo adapita kunkhondowo, Lemba la cilamuloco Yehova analamulira Mose ndi ili:

Werengani mutu wathunthu Numeri 31