Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 26:63-65 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

63. Iwo ndiwo amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eleazara wansembe, amene anawerenga ana a Israyeli m'zidikha za Moabu ku Yordano pafupi pa Yeriko.

64. Koma pakati pao panalibe mmodzi wa iwo amene anawerengedwa ndi Mose ndi Aroni wansembe, amene anawerenga ana a Israyeli m'cipululu ca Sinai.

65. Popeza Yehova adanena za iwowa, Adzafatu m'cipululu. Ndipo sanatsalira mmodzi wa iwowa koma Kalebi mwana wa Yefune, ndi Yoswa mwana wa Nuni.

Werengani mutu wathunthu Numeri 26