Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 26:3-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Pamenepo Mose ndi Eleazara wansembe ananena nao m'zidikha za Moabu pa Yordano kufupi ku Yeriko, ndi kuti,

4. Awawerenge kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu; monga Yehova anawauza Mose ndi ana a Israyeli, amene adaturuka m'dziko la Aigupto.

5. Rubeni, ndiye woyamba kubadwa wa Israyeli; ana amuna a Rubeni ndiwo: Hanoki, ndiye kholo la banja la Ahanoki; Palu, ndiye kholo la banja la Apalu;

6. Hezeroni, ndiye kholo la banja la Ahezeroni; Karimi, ndiye kholo la banja la Akarimi.

7. Iwo ndiwo mabanja a Arubeni; owerengedwa ao ndiwo zikwi makumi anai mphambu zitatu kudza mazana asanu ndi awiri mphambu makumi atatu,

8. Mwana wamwamuna wa Palu ndiye Eliyabu.

9. Ndi ana a Eliyabu: Nemueli, ndi Datani ndi Abiramu. Iwo ndiwo Datani ndi Abiramu omwe aja oitanidwa a khamu, amene anatsutsana ndi Mose ndi Aroni mu msonkhano wa Kora, mula anatsutsana ndi Yehova;

10. ndipo dziko linayasama pakamwa pace, ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, pakufa msonkhano uja; muja mote unaononga amuna mazana awiri ndi makumi asanu, nakhala iwo cizindikilo.

11. Koma sanafa ana amuna a Kora.

12. Ana amuna a Simeoni monga mwa mabanja ao ndiwo: Nemueli, ndiye kholo la banja la Anemueli; Yamini, ndiye kholo la banja la Ayamini; Yakini, ndiye kholo la banja la Ayakini;

13. Zera, ndiye kholo la banja la Azera; Sauli, ndiye kholo la banja la Asauli.

14. Iwo ndiwo mabanja a Asimeoni, zikwi makumi awiri mphambu ziwirikudzamazana awiri.

15. Ana amuna a Gadi monga mwa mabanja ao ndiwo: Zefoni, ndiye kholo la banja la Azefoni; Hagi, ndiye kholo la banja la Ahagi; Suni, ndiye kholo la banja la Asuni;

16. Ozini, ndiye kholo la banja la Aozini; Eri, ndiye kholo la banja la Aeri;

17. Arodi, ndiye kholo la banja la Aarodi; Areli, ndiye kholo la banja la Aareli.

18. Iwo ndiwo mabanja a ana a Gadi, monga mwa owerengedwa ao, zikwi makumi anai ndi mazana asanu.

19. Ana amuna a Yuda, ndiwo Eri ndi Onani; ndipo Eri ndi Onani anamwalira m'dziko la Kanani.

20. Ndipo ana a Yuda monga mwa mabanja ao ndiwo: Sela, ndiye kholo la banja la Asela; Perezi, ndiye kholo la banja la Aperezi; Zera, ndiye kholo la banja la Azera.

21. Ndipo ana a Perezi ndiwo: Hezeroni, ndiye kholo la banja la Ahezeroni; Hamuli, ndiye kholo la banja la Ahamuli.

22. Iwo ndiwo mabanja a Yuda monga mwa owerengedwa ao, zikwi makumi asanu ndi awiri mphambu zisanu ndi cimodzi kudza mazana asanu.

23. Ana amuna a Isakara monga mwa mabanja ao ndiwo: Tola, ndiye kholo la banja la Atola; Puva, ndiye kholo la banja la Apuni;

Werengani mutu wathunthu Numeri 26