15. Ana amuna a Gadi monga mwa mabanja ao ndiwo: Zefoni, ndiye kholo la banja la Azefoni; Hagi, ndiye kholo la banja la Ahagi; Suni, ndiye kholo la banja la Asuni;
16. Ozini, ndiye kholo la banja la Aozini; Eri, ndiye kholo la banja la Aeri;
17. Arodi, ndiye kholo la banja la Aarodi; Areli, ndiye kholo la banja la Aareli.
18. Iwo ndiwo mabanja a ana a Gadi, monga mwa owerengedwa ao, zikwi makumi anai ndi mazana asanu.
19. Ana amuna a Yuda, ndiwo Eri ndi Onani; ndipo Eri ndi Onani anamwalira m'dziko la Kanani.