Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 22:7-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo akuru a Moabu ndi akuru a Midyani anamuka ndi mphotho za maula m'dzanja lao; anadza kwa Balamu, nanena naye mau a Balaki.

8. Ndipo ananena nao, Mugone kuno usiku uno, ndidzakubwezerani mau, monga Yehova adzanena ndi ine; pamenepo mafumu a Moabu anagona ndi Balamu.

9. Ndipo Mulungu anadza kwa Balamu, nati, Anthu awa ali ndi iwe ndiwo ayani?

10. Ndipo Balamu anati kwa Mulungu, Balaki mwana wa Zipori mfumu ya Moabu, anatumiza kwa ine, ndi kuti,

11. Taonani, anthu awa adaturuka m'Aigupto aphimba nkhope ya dziko, idzatu unditembererere awa; kapena ndidzakhoza kulimbana nao nkhondo, ndi kuwapitikitsa.

12. Koma Mulungu anati kwa Balamu, Usapita nao; usatemberera anthuwa; pakuti adalitsika.

13. Ndipo Balamu anauka m'mawa, nati kwa akalonga a Balaki, Mukani ku dziko lanu; popeza Yehova andikaniza kuti ndisapite nanu,

14. Pamenepo akalonga a Moabu ananyamuka, nafika kwa Balaki, nati, Alikukana Balamu kudza nafe.

15. Koma Balaki anaonjeza kutumanso akalonga, ocuruka, ndi omveka koposa awa.

16. Ndipo anadza kwa Balamu, nati kwa iye, Atero Balaki mwana wa Zipori, Pasakhaletu cinthu cakukuletsa kudza kwa ine;

Werengani mutu wathunthu Numeri 22