Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 21:8-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Pamenepo Yehova anati kwa Mose, Upange njoka yamoto; nulike pa mtengowace; ndipo kudzali, kuti onse olumwa, akuipenya njokayo, adzakhala ndi moyo.

9. Ndipo Mose anapanga njoka yamkuwa, naiika pamtengo; ndipo kunali, njoka itamluma munthu ali yense, nakapenyetsetsa iye pa njoka yamkuwa, nakhala ndi moyo.

10. Pamenepo ana a Israyeli anayenda ulendo, namanga mahema m'Oboti.

11. Ndipo anacoka ku Oboti, namanga mahema ku Iyebarimu, m'cipululu cakuno ca Moabu, koturukira dzuwa.

Werengani mutu wathunthu Numeri 21