Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 21:29-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Tsoka kwa iwe, Moabu!Mwaonongeka, anthu a Kemosi inu,Anapereka ana ace amuna opulumuka,Ndi ana ace akazi akhale ansinga,Kwa Sihoni mfumu ya Aamori.

30. Tinawagwetsa; Hesiboni waonongeka kufikira ku Diboni,Ndipo tinawapululutsa kufikira ku Nofa,Ndiwo wakufikira ku Medeba.

31. Comweco Israyeli anakhala m'dziko la Aamori.

32. Ndipo Mose anatumiza anthu akazonde Yazere, nalanda miraga yace, napitikitsa Aamori a komweko.

33. Ndipo anatembenuka nakwera kudzera njira ya ku Basanu; ndipo Ogi mfumu ya ku Basana anaturuka kukumana nao, iye ndi anthu ace onse, kudzacita nao nkhondo ku Edreyi.

34. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Usamuopa; popeza ndampereka m'manja mwako, iye ndi anthu ace onse, ndi dziko lace; umcitire monga umo unacitira Sihoni mfumu ya Aamori anakhalayo ku Hesiboni.

Werengani mutu wathunthu Numeri 21