Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 16:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo anasonkhana motsutsana pa Mose ndi Aroni, nanena nao, Mukula mphamvu inu, pakuti khamu lonse nlopatulika, onsewa, ndipo Yehova ali pakati pao; mudzikuza bwanji pa msonkhano wa Yehova?

4. Pamene Mose anamva ici anagwa nkhope yace pansi;

5. nanena ndi Kora ndi khamu lace lonse, ndi kuti, M'mawa Yehova adzatizindikiritsa anthu ace ndi ayani, wopatulika ndani, amene adzamsendeza pafupi pa iye; ndi iye amene anamsankha adzamsendeza pafupi pa iye.

6. Citani ici; dzitengereni mbale za zofukiza, Kora, ndi khamu lace lonse;

7. nimuikemo moto, muikenso cofukiza pamenepo, pamaso pa Yehova, mawa; ndipo kudzali kuti amene Yehova amsankha, wopatulika ndiye; mwakula mphamvu, inu ana a Levi.

8. Ndipo Mose ananena ndi Kora, Tamvani tsono, inu ana a Levi;

Werengani mutu wathunthu Numeri 16