Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 16:18-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Potero munthu yense anatenga mbale yace yofukizamo, naikamo moto, naikapo cofukiza, naima pa khomo la cihema cokomanako pamodzi ndi Mose ndi Aroni.

19. Ndipo Kora anasonkhanitsa khamu lonse mopikisana nao ku khomo la cihema cokomanako; ndipo ulemerero wa Yehova unaoneka kwa khamu lonse.

20. Ndipo Yehova ananena ndi Mose ndi Aroni, nati,

21. Dzipatu, leni pakati pa khamu lino, kuti ndi wathe m'kamphindi.

22. Ndipo anagwa nkhope zao pansi, nati, Mulungu, ndinu Mulungu wa mizimu ya anthu onse, walakwa munthu mmodzi, ndipo kodi mukwiya nalo khamu lonse?

23. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

24. Nena ndi khamulo, ndi kuti, Kwerani kucoka pozungulira mahema a Kora, Datani, ndi Abiramu.

25. Ndipo Mose anauka namuka kwa Datani ndi Abiramu; ndi akuru a Israyeli anamtsata.

Werengani mutu wathunthu Numeri 16