Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 15:3-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. ndipo mukakonzera Yehova nsembe yamoto, nsembe yopsereza, kapena yophera, pocita cowinda ca padera, kapena nsembe yaufulu, kapena nsembe ya pa nyengo zanu zoikika, kumcitira Yehova pfungo lokoma, la ng'ombe kapena nkhosa;

4. pamenepo iye wobwera naco copereka cace kwa Yehova, azibwera nayo nsembe yaufa, limodzi la magawo khumi la ufa wosalala, wosanganiza ndi limodzi la magawo anai la bini la mafuta;

5. ndipo uzikonzera nsembe yopsereza kapena yophera, vinyo wa nsembe yothira, limodzi la magawo anai la bini, ukhale wa mwana wa nkhosa mmodzi.

6. Kapena ukonzere nkhosa yamphongo nsembe yaufa, awiri mwa magawo khumi a ufa wosalala, wosanganiza ndi mafuta, limodzi la magawo atatu la bini.

7. Ndipo ubwere naye vinyo wa nsembe yothira, limodzi la magawo atatu la bini, acitire Yehova pfungo lokoma.

8. Ndipo pamene mukonza ng'ombe ikhale nsembe yopsereza, kapena yophera, kucita cowinda ca padera, kapena ikhale nsembe yoyamika ya Yehova;

9. abwere nayo, pamodzi ndi ng'ombeyo, nsembe ya ufa wosalala, atatu mwa magawo khumi wosanganiza ndi mafuta, limodzi la magawo awiri la bini.

10. Ndipo ubwere naye vinyo wa nsembe yothira limodzi la magawo awiri la hini, ndiye nsembe yamoto ya pfungo: lokoma, ya Yehova.

11. Kudzatero ndi ng'ombe iri yonse, kapena nkhosa yamphongo iri yonse, kapena mwana wa nkhosa ali yense, kapena mwana wa mbuzi ali yense.

12. Monga mwa kuwerenga kwace kwa izi muzikonza, muzitero ndi yonse monga mwa kuwerenga kwace.

13. Onse akubadwa m'dzikomo acite izi momwemo, pobwera nayo kwa Yehova nsembe yamoto ya pfungo lokoma.

14. Ndipo akakhala nanu mlendo, kapena ali yense wakukhala pakati pa inu mwa mibadwo yanu, nakacitira Yehova nsembe yamoto ya pfungo lokoma; monga mucita inu, momwemo iyenso,

15. Kunena za khamu, pakhale lemba limodzi kwa inu, ndi kwa mlendo wakukhala kwanu, ndilo lemba losatha mwa mibadwo yanu; monga mukhala inu, momwemo mlendo pamaso pa Yehova.

16. Pakhale cilamulo cimodzi ndi ciweruzo cimodzi kwa inu ndi kwa mlendo wakukhala kwanu.

Werengani mutu wathunthu Numeri 15