Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 15:28-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Ndipo wansembe acite comtetezera munthu wakulakwa, osalakwa dala pamaso pa Yehova, kumcita comtetezeraj ndipo adzakhululukidwa.

29. Kunena za wobadwa m'dziko mwa ana a Israyeli, ndi mlendo wakukhala pakati pao, mukhale naco cilamulo cimodzi kwa iye wakucita kanthu kosati dala.

30. Koma munthu wakucita kanthu dala, ngakhale wobadwa m'dziko kapena mlendo, yemweyo acitira Yehova mwano; ndipo munthuyo amsadze pakati pa anthu a mtundu wace.

31. Popeza ananyoza mau a Yehova, nathyola lamulo lace; munthuyu amsadze konse; mphulupulu yace ikhale pa iye.

32. Ndipo pokhala ana a Israyeli m'cipululu, anapeza munthu wakufuna nkhuni tsiku la Sabata.

33. Ndipo amene adampezawo alinkufuna nkhuni anabwera naye kwa Mose ndi Aroni, ndi kwa khamu lonse.

Werengani mutu wathunthu Numeri 15