Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 14:16-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Popeza Yehova sanakhoza kuwalowetsa anthu awa m'dziko limene anawalumbirira, cifukwa cace anawapha m'cipululu.

17. Ndipo tsopano, ikuletu mphamvu ya Mbuye wanga, monga mudanena, ndi kuti,

18. Yehova ndiye wolekereza, ndi wa cifundo cocuruka, wokhululukira mphulupulu ndi kulakwa, koma wosamasula woparamula; wakuwalanga ana cifukwa ca mphulupulu ya atate ao, kufikira mbadwo wacitatu ndi wacinai.

19. Khululukiranitu mphulupulu ya anthu awa, monga mwa cifundo canu cacikuru, ndi monga mudalekerera anthu awa, kuyambira Aigupto kufikira tsopano.

20. Ndipo Yehova anati, Ndakhululukira monga mwa mau ako:

21. koma ndithu, pali Ine, dziko lonse lapansi lidzadzazidwa ndi ulemerero wa Yehova;

22. popeza anthu onse awa amene adaona ulemerero wanga, ndi zizindikilo zanga, ndidazicita m'Aigupto ndi m'cipululu, koma anandiyesa Ine kakhumi aka, osamvera mau anga;

23. sadzaona dzikoli ndidalumbirira makolo ao, ngakhale mmodzi wa iwo akundinyoza Ine, sadzaliona;

24. koma mtumiki wanga Kalebi, popeza anali nao mzimu wina, nanditsata monsemo, ndidzamlowetsa iyeyu m'dziko muja analowamo; ndi mbeu zace zidzakhala nalo.

25. Koma Aamaleki ndi Akanani akhala m'cigwamo; tembenukani mawa, nimumke ulendo wanu kucipululu, njira ya ku Nyanja Yofiira.

26. Ndipo Yehova ananena kwa Mose ndi Aroni, nati,

27. Ndileke khamu loipa ili lakudandaula pa Ine kufikira liti? Ndidamva madandaulo a ana a Israyeli, amene amandidandaulira.

28. Nunene nao, Pali Ine, ati Yehova, ndidzacitira inu ndithu monga mwanena m'makutu mwanga;

29. mitembo yanu idzagwa m'cipululu muno; ndi owerengedwa anu onse, monga mwa kuwerenga kwanu konse, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, akudandaula pa Ine;

30. simudzalowa inu m'dzikolo, ndinakwezapo dzanja langa kukukhalitsani m'mwemo, koma Kalebi mwana wa Yefune, ndi Yoswa mwana wa Nuni ndiwo.

31. Koma makanda anu, amene munanena za iwowa kuti adzakhala cakudya, amenewo ndidzavalowetsa, ndipo adzadziwa dzikolo mudalikana.

32. Koma inu, mitembo yanu idzagwa m'cipululu muno.

33. Ndipo ana anu adzakhala oyendayenda m'cipululu zaka makumi anai, nadzasenza kupulukira kwanu, kufikira mitembo yanu yatha m'cipululu.

34. Monga mwa kuwerenga kwa masiku amene munazonda dziko, masiku makumi anai, tsiku limodzi kuwerenga caka cimodzi, mudzasenza mphulupulu zanu, zaka makumi anai, ndipo mudzadziwa kuti ndaleka lonjezano langa.

Werengani mutu wathunthu Numeri 14