Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 11:9-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo pakugwa mame pacigono usiku, mana anagwapo.

10. Ndipo Mose anamva anthu alikulira m'mabanja ao, yense pakhomo pa hema wace; ndipo Yehova anapsa mtima ndithu, ndipo kudamuipira Mose.

11. Ndipo Mose anati kwa Yehova, Munacitiranji coipa mtumiki wanu? ndalekeranii kupeza ufulu pamaso panu, kuti muika pa ine katundu wa anthu awa onse?

12. Kodi ndinaima nao anthu awa onse? kodi ndinawabala, kuti munene nane, Uwayangate ngati mlezi afukata khanda, kumka nao ku dzikolo mudalumbirira makolo ao?

13. Ndidzaiona kuti nyama yakuwapatsa anthu awa onse? pakuti amalirira ine, ndi kuti, Tipatseni nyama, tidye.

14. Sinditha kuwasenza anthu awa onse ndekha, pakuti andilemera ine.

15. Ndipo ngati mundicitira cotero, mundiphetu tsopano apa, ngati ndapeza ufulu pamaso panu, ndisayang'ane tsoka langa.

16. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Undisonkhanitsire amuna makumi asanu ndi awiri mwa akuru a Israyeli, amene uwadziwa kuti ndiwo akuru a anthu, ndi akapitao ao; nubwere nao ku cihema cokomanako, kuti aimeko pamodzi ndi iwe.

Werengani mutu wathunthu Numeri 11