Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 10:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Mukaliza cokweza, ayende a m'zigono za kum'mawa.

6. Mukalizanso cokweza, a m'zigono za kumwela ayende; alize cokweza pakumuka.

7. Pomemeza msonkhano mulize, wosati cokweza ai.

8. Ana amuna a Aroni, ansembe, ndiwo aziliza malipenga; ndipo akhale kwa inu lemba losatha ku mibadwo yanu.

9. Ndipo pamene mupita kunkhondo m'dziko lanu kucita nkhondo pa mdani wakusautsa inu, mulize cokweza ndi malipenga; ndipo Yehova Mulungu wanu adzakumbukila inu, nadzakupulumutsani kwa adani anu.

10. Momwemo tsiku lakukondwera inu, ndi nyengo zoikidwa zanu, ndi poyamba miyezi yanu, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza, ndi pa nsembe zanu zoyamika; ndipo akhale kwa inu cikumbutso pamaso pa Mulungu wanu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

11. Ndipo kunacitika, caka caciwiri, mwezi waciwiri, tsiku la makumi awiri la mweziwo, kuti mtambo unakwera kucokera kwa kacisi wa mboni.

Werengani mutu wathunthu Numeri 10