Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 10:2-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Dzipangire malipenga awiri asiliva; uwasule mapangidwe ace; ucite nao poitana khamu, ndi poyendetsa a m'zigono.

3. Akaliza, khamu lonse lisonkhane kuli iwe ku khomo la cihema cokomanako,

4. Akaliza limodzi, pamenepo akalonga, akuru a zikwi a m'Israyeli, azisonkhana kuli iwe.

5. Mukaliza cokweza, ayende a m'zigono za kum'mawa.

6. Mukalizanso cokweza, a m'zigono za kumwela ayende; alize cokweza pakumuka.

7. Pomemeza msonkhano mulize, wosati cokweza ai.

8. Ana amuna a Aroni, ansembe, ndiwo aziliza malipenga; ndipo akhale kwa inu lemba losatha ku mibadwo yanu.

9. Ndipo pamene mupita kunkhondo m'dziko lanu kucita nkhondo pa mdani wakusautsa inu, mulize cokweza ndi malipenga; ndipo Yehova Mulungu wanu adzakumbukila inu, nadzakupulumutsani kwa adani anu.

Werengani mutu wathunthu Numeri 10