Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Numeri 10:1-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2. Dzipangire malipenga awiri asiliva; uwasule mapangidwe ace; ucite nao poitana khamu, ndi poyendetsa a m'zigono.

3. Akaliza, khamu lonse lisonkhane kuli iwe ku khomo la cihema cokomanako,

4. Akaliza limodzi, pamenepo akalonga, akuru a zikwi a m'Israyeli, azisonkhana kuli iwe.

5. Mukaliza cokweza, ayende a m'zigono za kum'mawa.

6. Mukalizanso cokweza, a m'zigono za kumwela ayende; alize cokweza pakumuka.

7. Pomemeza msonkhano mulize, wosati cokweza ai.

8. Ana amuna a Aroni, ansembe, ndiwo aziliza malipenga; ndipo akhale kwa inu lemba losatha ku mibadwo yanu.

9. Ndipo pamene mupita kunkhondo m'dziko lanu kucita nkhondo pa mdani wakusautsa inu, mulize cokweza ndi malipenga; ndipo Yehova Mulungu wanu adzakumbukila inu, nadzakupulumutsani kwa adani anu.

10. Momwemo tsiku lakukondwera inu, ndi nyengo zoikidwa zanu, ndi poyamba miyezi yanu, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza, ndi pa nsembe zanu zoyamika; ndipo akhale kwa inu cikumbutso pamaso pa Mulungu wanu; Ine ndine Yehova Mulungu wanu.

11. Ndipo kunacitika, caka caciwiri, mwezi waciwiri, tsiku la makumi awiri la mweziwo, kuti mtambo unakwera kucokera kwa kacisi wa mboni.

12. Ndipo ana a Israyeli anayenda monga mwa maulendo ao, kucokera m'cipululu ca Sinai; ndi mtambo unakhala m'cipululu ca Parana.

13. Potero anayamba ulendo wao monga mwa mau a Yehova ndi dzanja la Mose.

14. Ndipo anayamba kuyenda a mbendera ya cigono ca ana a Yuda monga mwa magulu ao; woyang'anira gulu lace ndiye Nahesoni mwana wa Aminadabu.

15. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Isakara panali Netaneli mwana wa Zuwara.

16. Ndi pa gulu la pfuko la ana a Zebuloni panali Eliyabu mwana wa Heloni.

17. Ndipo anagwetsa kacisi; ndi ana a Gerisoni, ndi ana a Merari, akunyamula kacisi, anamuka naye.

Werengani mutu wathunthu Numeri 10